Published 3 years ago in Other
malawitunesads malawitunesads malawitunesads malawitunesads
  • 517
  • 919
  • 1
  • 0
  • 4
  • 0
  • 0

Download Robert Chiwamba - Mbiri Safuta

Lyrics

MBIRI SAFUTA

Ngwazi Prof. Bingu wa Mutharika adali wakulu

Olo utapita kunja nkhani yake ukayipeza
Kutseka maso ako pogona mbiri yake ukayilota
Kuthawira kumaiko akutali, m'mabuku akumeneko za masomphenya ake ukazikumana
Mbiri yadziko lino ndi sanza opanda malemu Professor Bingu wa Mutharika,
Ngwazi yachiwiri ya pfuko la Nyasaland, chitsulo chanjanji, nthetsa makani anzungu Katswiri.

Anayankhulako m'modzi mwa atsogoleri athu padzana
Kuti vuto la Amalawi ambirife sitichedwa kuyiwala
Koma lero pamene tukumbukira Mapwiya Mulhupale sindikulorani kuti muyiwale
Kuti mukangosamba nkulowa munsewu wa Chitipa Karonga mwalowa mu ntchito za manja ake
Ndithu mukangopenya munthu akudumphadumpha amusankhira ku MUST dziwani akujowelajowela zipatso za mifuleni ya thukuta lake
Akangoti ndimagwira ntchito kunyumba yamalamulo dziwani amabindikira mu nyumba zomwe anamanga ndi luntha lake

Nsanje sachitira akufa, mbiri ilibe Dastala, M'kunena kwa achinyamata alero Ngwazi Professor Lorani ntchito za manja anga zindichitire umboni aja anali dada

Anamangira Kamuzu nyumba yogonamo kwamuyaya yaulemu
Uku timakuti chitsulo kulemekeza chitsulo chinzake
Sanamvere Mzungu pomukaniza kuyambitsa feteleza otchipa, anamuyambitsa njala yonse balala
Uku timakutcha kudziwa chomwe ukuchita
Potumbwa Edzi anagawa ma ARV aulere imfa zodza ndi iyo Red Card Lakata
Uwu timautcha utsogoleri okonda anthu

Ngwazi Professor tiyende pamodzi ndi mtima umodzi aja sanali size yanu
Ngwazi Professor  Bingu Wamutharika uja sungamamuyerekeze ntatsogoleri tamabungwe tongopanga phokoso mmawayilesiti
Ngwazi Prof. belu suyimba uli pakaliyala aja mbewu yawo anasiya kupanga

Moti ndunena pano sindingayiwale kuwauza ana anga kuti chinasesa mavote Chitipa to nsanje chokhachokha  ana amuna bambo
Zonse ndege ndi ma tractor a green belt zinasowetsedwa zija zinali thukuta la kulimbika mtima kwake akatundu bwana
Mayi anu achira? Kuchipatala cha Nkhotakota kaya Nkhatabay wo achilira mu nyumba zomwe anamanga kudzera mmasomphenya ake

Ndale tazisiyani, ufiti musamatambe masana, nsanje sachitira akufa perekani ulemu kwa Professor Bingu Katakwe

Anagumula nyumba zonse zomangidwa mosatsata malamulo, kuthamangitsa ma vendor munsewu, kukana mathanyula kuliri kuveka ma driver ndi ma conductor a ma minibus Uniform

Uku timakutcha kuswa kuswa

Tutitu anathotha Kazembe wa angerezi, kukana kugwetsa mphavu yakwacha, kulili kuopseza kuti athamangitsa timakampani togula fodya, fodya kukweleratu mtengo

Uku timakuti kusenda kusenda

Eish anawauza apolisi wakuba wamfuti Shoot to Kill umbava onse thii lakata
Uwu timautcha utsogoleri wachitetezo

Ngwazi Professor Shoot to Kill aja anali mfumu ya kuswa kuswa
Ngwazi Prof uja monga inenso ankadziwa kuti apolisi ngofunikira osamawaphweketsa
Ngwazi achiwiri aja anali makolo

Zofooka mu ulamuliro wawo osalephera mwana okonzedwa pa Poly, kulili anthu otsogozedwa kulichete pa 20 July

Pepani olira pepani

Zolakwika zinalipodi, anyamata achipani ozungulira ndi zikwanje, mafuta, shuga, magetsi ndalama zakunja kusowa
koma ndindani amene anabadwa mwankazi alibe zofowoka ndiyankheni?

Ulamuliro wa Ngwazi Prof. Bingu Wa Mutharika sunali wa angelo
Ngwazi Prof Bingu Wa Mutharika monga inuyo ndi akazanuwonso anali ndi zofooka
Zofowoka za Ngwazi Prof Bingu Wamutharika zinali zochepa tikayerekeza ndi chake chitukuko komabe sitingazipeputse pepani olira pepani

Nde lero pamene zilumika zapitapo chipezereni ufulu ozisaukitsa tokhawu
Nduti lero, pamene amalawi ambiri akubadwabe kukula mpaka kufa mumdima wa umphawi wadzaoneni
Sitingayiwale  Professor Bingu wa Mutharika Malemu
Limodzi ndi makosana ena amene anayesetsako kuyasa nyali mumdima wathu
Achina Mayi Anastanzia Msosa ndi mayi Ethel Mutharika Malemu.
Bwana Dr. Chifundo Kachali ndi bambo Nyakwawa Usiwa Usiwa malemu
Zikomo chifukwa cha chilichonse munachitira Malawi
Yakanika ndakatulo kufotokoza zonse  zitukuko za Ngwazi yachiwiriyi zachulukitsa
Koma ngati pali tsache, ninkheni nkasese  mwaulemu kumpumulo wabata
Ngati pali chitchetcho patseni nkatchetche panyumba yotsiriza yabambo pasamele udzu
Chitsime chimadziwikadi kuya madzi pouma
Ngwazi Professor Bingu Wa Mutharika uja ankatikonda
Ngwazi prof Bingu uja sitinamumvetse
Ngwazi Prof. Bingu uja adali wakulu
Mbiri safuta.

:
/ :

Queue

Clear